Malawi Broadcasting Corporation
Business Local News Nkhani

MUSCCO yachita phindu lokwana K82 billion

Bungwe la Malawi Union of Savings and Credit Cooperatives (MUSCCO) lati chuma chama SACCO tsopano chakwana K82 billion chaka chino chokha kuchokera kwa mamembala okwana 239,000 m’dziko lino.

Kutsatira izi, m’modzi mwa akuluakulu a bungweli, a Daniel Infa, amema aMalawi kuti adzisungitsa ndalama ku nthambi zawo pofuna kuchulukitsa makobili.

Izi zidadziwika loweruka pa msonkhano wa pa chaka wa nthambi ya Kasupe SACCO mu mzinda wa Lilongwe.

Mtsogoleri wawo, a Philip Kaingo, anatsimikiza kuti iwo akuchita phindu chifukwa akwanitsa kuchulutsa ndalama zawo, kuphatikizirapo katundu, zomwe ndi zokwana K254 million kuchoka pa K209 million.

A Kaingo anaonjezerapo kunena kuti padakali pano akwanitsa kutorera ndalama zokwana K18 million pa mamembala okwana 431.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Chimbale chatsopano ndichothokoza Mulungu — Thuya

Paul Mlowoka

Parliament intervention boosts Ombudsman ruling compliance

MBC Online

VP to attend Human Resource Society of Malawi AGM

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.