Malawi Broadcasting Corporation
News Nkhani

Muli ndi ufulu olowa chipani chomwe mwafuna – Brown Mpinganjira

Mmodzi mwa akuluakulu a chipani cha Malawi Congress Party (MCP) m’chigawo chakum’mwera, a Brown Mpinganjira, apempha anthu a m’boma la Thyolo kuti asamaope kapena kuopsezedwa ndi anthu a zipani zina akafuna kulowa chipani cha MCP.

A Mpinganjira amayankhula izi kwa Bvumbwe m’bomali pamene amapereka zovala za makaka a chipani cha MCP monga ma T-Shirt ndi nsalu.

Iwo anapitirizanso kunena kuti dziko la Malawi ndi lazipani zambiri ndipo anthu ali ndi ufulu olowa chipani chomwe angafune.

A Mpinganjira apemphanso anthu kuti adzavotere  aphungu a MCP mu chisankho cha mchaka cha 2025.

 

 

By Alufisha Fischer.

Related posts

Mpikisano wa BT 42.195 KM Race ndi waulele

Romeo Umali

UK supports Malawi’s education sector with K90BN

Romeo Umali

Snr Chief Kapoloma to be laid to rest today

Alinafe Mlamba
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.