Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Local News Nkhani

‘Mukapezeka ndi Chamba mumangidwa’

Apolisi ku Karonga achenjeza kuti aliyense opezeka ndi fodya wamkulu (Chamba) adzimangidwa.

Iwo anena zimenezi atamanga a Michael Chiwaya azaka 31 powaganizira kuti apezeka ndi Chamba cha makilogiramu 38 mosavomerezeka ndi boma.

Ofalitsankhani ku polisi ya Karonga, a Margret Msiska, ati oganiziridwayu pa 09 October 2024 anapezeka ndi zikwama zitatu ndi thumba la pulasitiki pa njinga zomwe akuti zimaoneka mokayikitsa ndipo wapolisi yemwe anaona izi anayamba kufufuza ndipo anapeza chambachi.

A Chiwaya aonekera kubwalo la milandu posachedwepa poyankha mlandu opezeka ndi chamba popanda chilolezo.

Iwo amachokera m’mudzi wa Mpeta kudera la Mfumu Kamphambale m’boma la Nkhotakota.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

MBC rolls out Ngwe Ngwe Ngwe project open days

MBC Online

A Malawi adekhe pamene boma likumanganso misewu yolimba – Hara

Madalitso Mhango

Ntchito yofufuza ndege m’dziko la Russia yayamba

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.