Malawi Broadcasting Corporation
Development Local News Nkhani

Khonsolo ya Mzuzu ikufuna K2.4BN

Khonsolo ya mzinda wa Mzuzu yati ikufuna kutolera ndalama zokwana K2.4 billion kuti igwire bwino ntchito zake zachitukuko,pansi pa ndondomeko yake ya chuma ya 2024/2025.

Mkulu wa khonsoloyi, a Gomezgani Nyasulu, amayankhula izi pokhazikitsa ntchito za chitukukozi.

“Ndalama izizi zitithandiza kuti tipange zambiri, kuphatikizapo ntchito yomanga zipinda za sukulu. Chaka chatha tinatolera ndalama yoposa 60 percent pa ndalama imene tinayerekeza,” atero a Nyasulu.

Akuluakulu ena a khonsoloyi anaonjezerapo kuti ndalamazi ziwathandizira kumalizitsa ntchito yokonza misewu komanso kuonetsetsa kuti mzinda wa Mzuzu ndi wa ukhondo.

Mfumu Thula inatsimikiza kuti imema anthu kuti adzipereka ndalama za misonkho, zotchedwa City Rates.

Olemba: Lovemore Shaba

Related posts

Ana aphunzitsidwe njira zodzitetezera ku nkhanza zogwiliridwa

Romeo Umali

Akonzetsa madesiki 65 ku Dowa

Romeo Umali

KAWALE HANDS OVER TRACTORS, FACILITIES TO COOPERATIVES

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.