Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Khonsolo ya mnzinda wa Zomba ili ndi Mfumu yatsopano

Khonsolo ya mnzinda wa Zomba yasankha a Christopher Jana adera la Mpira ngati mfumu yatsopano ya mnzindawu.

A Jana alowa mmalo mwa a Davie Maunde omwe akhala pa mpandowu kuchoka chaka cha 2021 atasankhidwa mmwezi wa December mchakacho.

A Anthony Gonani ndiye wachiwiri kulowa mmalo mwa a Munira Bakali a Likangala ward.

A Jana anakhalaponso pa udindowu mchaka cha 2018 kufika 2020 pomwe khansala Benson Bula anatenga udindowu kufikira 2021.

Related posts

Tsogolo la mlandu wa a Mbedza lioneka masana ano

Romeo Umali

“Osanyoza anthu achikulire” — Chakwera

Romeo Umali

Alexander ‘Cage’ Likande wamwalira

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.