Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Sports Sports

Alexander ‘Cage’ Likande wamwalira

Katswiri wa nkhonya m’dziko muno, Alexander ‘Cage’ Likande, wamwalira m’bandakucha wa lero pangozi ya njinga yamoto yomwe inaombana ndi galimoto.

Malinga ndi zimene akunena mnzake Byson Gwayani, Likande anachita ngoziyi dzulo usiku akuchokera ku Area 36 mu mzinda wa Lilongwe kumene kunali masewero a nkhonya.

Malipoti akuti atathamangira naye ku chipatala cha Kamuzu Central kuti akalandire thandizo, iye anamwalira.

Mwambo wa maliro a Likande akhale akuwulengeza ndi a kubanja komanso adindo a bungwe loyendetsa nkhonya m’dziko muno la MPBCB.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Mussa Ajibu asambitsa chokweza Vissah

MBC Online

Tabitha ndi katswiri mbambande ku France

Emmanuel Chikonso

Community mourns late Shanil Dzimbiri

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.