Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Khonsolo ya mnzinda wa Lilongwe ikuchotsa zinyanyala usiku uno

Khonsolo ya mnzinda wa Lilongwe usiku uno ikugwira ntchito yosesa komanso kuchotsa zinyalala mu munzindawu.

Mfumu yamnzindawu, a Esther Sagawa, ndiyo ikutsogolera ntchitoyi yomwe yayambira ku City Centre.

Malinga ndi a Sagawa, adzigwira ntchitoyi usiku pofuna kuonetsetsa kuti ikuchitika moyenera ndipo ati azichita izi katatu pasabata iliyonse.

Iwo apempha eni ma shop munzindawu kuti akhale ndi motaila zinyalala ndicholinga choti ntchito yokonza mumnzindawu isamavute.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Talandira K6 miliyoni koma siyokwanira — Silver Strikers

Emmanuel Chikonso

Ochita bizinesi zing’onozing’ono apindula mu mgwirizano wa NBM ndi kampani zina

MBC Online

Bungwe la FAO lithandiza dziko la Malawi

Blessings Kanache
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.