Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Mwana wa Standard 5 wadzipha atamuletsa kuchita zibwenzi

Mtsikana wazaka 15, Eneles Namusanyo, yemwe anali sitandade 5, wadzipha pokwiya chifukwa chodzudzulidwa khalidwe la zibwenzi.

Ofalitsankhani zapolisi ku Mulanje, Innocent Moses, wati mtsikanayo anali pachibwenzi ndi mnyamata wina ndipo mayi ake atadziwa izi, anakhala naye pansi kumulangiza kuti asamachite khalidweli.Kenako mayiwo anachoka pakhomopo ndipo pobwera sanamupeze mwana wawoyo mpaka tsiku lotsatira.

Kutacha, anthu anamupeza atadzimangilira ku denga la nyumba yawo.

Malemuyu anali wa mmudzi wa Ngongondole, mfumu yaikulu Mabuka m’boma la Mulanje.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Stakeholders bang heads on tobacco smoke control

Yamikani Simutowe

CDC urges African countries to adopt One Health approach

Doreen Sonani

Innovations can tackle Malawi’s challenges — Chakwera

Eunice Ndhlovu
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.