Malawi Broadcasting Corporation
Health Local Local News Nkhani

Gawo loyamba lomanga chipatala cha Mponela Community likutha

Mkulu oyang’anira zomangamanga ku unduna wa zaumoyo, Dr Sanderson Kuyeli, wati gawo loyamba pantchito yomanga chipatala cha Mponela Community m’boma la Dowa latsala pang’ono kutha.

Iwo ayankhula izi atayendera chipatalachi pamodzi ndi adindo amu ofesi ya mtsogoleri wa dziko lino ndi maunduna.

Chipatala cha Mponela Community chikuyembekezeka kuchepetsa kuchulukana kwa anthu ofuna thandizo pa chipatala cha boma ku Dowa.

Chipatalachi chikhala ndi zipinda zochita opaleshoni, zipinda zogona anthu odwala momwe mukhale makama 100, nyumba za anthu ogwila ntchito okwana 46 komanso nyumba yachisoni, ndi zina zambiri.

“Malo ano pamene pali chipatala chino tikukhulupilira kuti chikatha chidzathandiza ngakhale anthu achita ngozi mu msewu wa M1, umene panopa boma likukonzanso,” Dr Kuyeli anatero.

Iwo anawonjezeranso kuti unduna wawo ukukonza zomalizitsa zipatala zimene ntchito yomanga idayamba yayima monga chipatala cha Chikapa ku Machinjiri munzinda wa Blantyre.

Print Friendly, PDF & Email

Author

  • Mayeso Chikhadzula joined MBC in 2006, he's an Investigative Journalist and Principal Reporter. He's also a News Anchor, Presenter, and producer.

Related posts

Retired nurse assisted after appearing on Reach Out and Touch

MBC Online

Nkhata Bay targets more than 5,000 in phase two of supplementary registration

Rabson Kondowe

Airtel Malawi loss stings minority shareholders

Justin Mkweu
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.