Malawi Broadcasting Corporation
Environment Local Local News Nkhani

DoDMA ifikira aliyense

Nthambi ya Department of Disaster Management Affairs (DoDMA) yatsimikizira anthu amene njala yawakhudza m’madera ovuta kufikako m’boma la Mangochi kuti ichita chotheka kuti anthu alandire chakudya.

Mkulu wa nthambiyi, a Charles Kalemba, anena izi ku Monkey-Bay kumene bungweli likutumiza chimanga kudzera pa sitima ya Ndunduma kuti akachipereke kwa anthu amene akuvutika ndi njala m’madera a mfumu yaikulu Makanjira komanso Luranga.

“Tikutumiza matumba a chimanga okwana 28,000 olemera ma kilogalamu 50 thumba lililonse ku mabanja amene akuvutika ndi njala,” a Kalemba adatsimikiza.

M’modzi mwa akuluakulu a ofesi yoona zaulimi m’bomalo, a Masautso Stanely Njolomole, ati mabanja 331,000 ndi amene akhudzidwa ndi vuto la njala ndipo pakadali pano mabanja 124,000 awafikira kale ndi thandizo la chakudya.

Olemba: Owen Mavula

Related posts

Bushiri’s case continues tomorrow

Romeo Umali

1MR wins 2024 MDF Tactical March and Combat Competition

Romeo Umali

A Kaliati akufuna kudzapikisana nawo pa udindo wa mtsogoleri wa UTM

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.