Malawi Broadcasting Corporation
Environment Local Local News Nkhani

DoDMA ifikira aliyense

Nthambi ya Department of Disaster Management Affairs (DoDMA) yatsimikizira anthu amene njala yawakhudza m’madera ovuta kufikako m’boma la Mangochi kuti ichita chotheka kuti anthu alandire chakudya.

Mkulu wa nthambiyi, a Charles Kalemba, anena izi ku Monkey-Bay kumene bungweli likutumiza chimanga kudzera pa sitima ya Ndunduma kuti akachipereke kwa anthu amene akuvutika ndi njala m’madera a mfumu yaikulu Makanjira komanso Luranga.

“Tikutumiza matumba a chimanga okwana 28,000 olemera ma kilogalamu 50 thumba lililonse ku mabanja amene akuvutika ndi njala,” a Kalemba adatsimikiza.

M’modzi mwa akuluakulu a ofesi yoona zaulimi m’bomalo, a Masautso Stanely Njolomole, ati mabanja 331,000 ndi amene akhudzidwa ndi vuto la njala ndipo pakadali pano mabanja 124,000 awafikira kale ndi thandizo la chakudya.

Olemba: Owen Mavula

Related posts

President Chakwera calls on religious leaders to support environmental restoration efforts

Romeo Umali

Viral Conjunctivitis outbreak hits Mchinji

Alinafe Mlamba

Apolisi athandiza pantchito yothana ndi mikangano yokhudza malo – Gumba

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.