Malawi Broadcasting Corporation
Health Local Local News Nkhani

Chipatala cha South Lunzu chikupempha thandizo

Chipatala cha South Lunzu m’boma la Blantyre chakonza ulendo wa ndawala mwezi wa mawa pofuna kupeza thandizo la ndalama zokwana K70 million zimene akufuna kuti agwiritse ntchito pokonza mavuto ambiri amene ali pa chipatalachi.

Wapampando wa komiti imene imayang’anira chipatalachi, a James Kalungwe, wati ndalamazi azigwiritsa ntchito pomanganso mpanda umene unagwa ndi namondwe Freddy komanso kukonza zimbudzi zimene zipangizo zake zinabedwa.

A Kalungwe anaonjezeranso kuti akufuna agwiritse ntchito ndalamazi pokhala ndi malo abwino otayira zinyalala komanso malo okhala odikilira odwala ndi kugula zitseko ndi mipando.

M’modzi mwa mzika za kuderali, amenenso ndi olembankhani, Deus Sandram, anati ndi okhudzidwa ndi momwe zithu zilili pa chipatalachi ndipo walonjeza kuthandizira kuti chipatalachi chipeze thandizo la ndalamazi.

 

Related posts

Moroccan Embassy in Malawi commemorates 46th Anniversary of Green March

McDonald Chiwayula

MANEPO hails passing of Older Persons’ Bill

Rabson Kondowe

UK supports Malawi’s education sector with K90BN

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.