Malawi Broadcasting Corporation
Africa Crime Local Local News Nkhani

BOMA LATHETSA MULANDU WA OSOKONEZA MDIPITI

Boma lathetsa mulandu wa anthu atatu omwe anawamanga chifukwa chosokoneza mdipiti wa mtsogoleri wa dziko lino pa HHI mu mzinda wa Blantyre.

Mkulu oimira boma pa milandu, a Masauko Chamkakala, watsimikiza zankhaniyi polankhula ndi wailesi za MBC.

Anthu atatu omwe amawazenga mulanduwu, a Pearson Chimimba a zaka 48, a Hector Ndawala a zaka 38, komanso a Lucy Namba a zaka 35, anawamanga patapita masiku angapo, anthu omwe anali pa maliro ndipo amachokera dera lina ku Ndirande ndipo amapita kukaika zobvuta kumanda a HHI, atalimbana ndi apolisi a pamsewu kuti adutse msewu pa malowa.

Mtsogoleri wa dziko lino anali paulendo opita ku Chileka kukakwera ndege kupita ku Democratic Republic of Congo (DRC) pamene anthuwa anachita chisokonezochi.

#mbcnewslive
#mbconlineservices
#mbcnewslive

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

How APM solved food puzzle in first 100 days

MBC Online

MBC HAILS TIES WITH CHINESE EMBASSY

McDonald Chiwayula

Dr Chakwera waphara vya nyifwa ya ngozi ya ndege

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.