Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Boma lagawa chimanga ku Zomba

Boma lakhazikitsa ntchito yogawa chimanga kwa mabanja pafupifupi 8000 amene njala inawakhudza munzinda wa Zomba.

Mwambo okhazikitsa ntchitoyi unachitika Lachitatu ku Matawale kwa mfumu yayikulu Mwambo munzindawu.

Mkulu wa khonsolo ya Zomba, Archangel Bakolo, wati thandizolo labwera mu nthawi yake kaamba kakuti anthu 17 mwa anthu 100 aliwonse ndi amene njala idawakhudza.

Kudzera ku DoDMA, boma likhala likupereka chimangacho kwa miyezi isanu kuchokera mwezi uno.

Banja lililonse likulandira thumba lolemera makilogalamu 50.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Mphunzitsi amumanga ataba ndalama za mayeso

Charles Pensulo

FAM launches 2023 National Women’s Football championship

Romeo Umali

Karonga United returns to winning ways

Rudovicko Nyirenda
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.