Malawi Broadcasting Corporation
Development Local News Nkhani

Anthu akondwa kuona sitima ikulunjika mtunda wa Mchinji

Anthu ambiri ku Area 25 ku Lilongwe ndi madera ozungulira m’mawa wa lero Loweluka anasonkhana pa mlatho wa Area 49 pa msewu wopita ku Nsungwi pomwe, kwanthawi yoyamba, sitima yoyesera komanso kukonza njanji yadutsa kulowera mtunda wa Mchinji, patatha zaka makumi atatu.

Anthuwa ayamika boma kuti zimenezi zithandiza kuti katundu wambiri adziyenda mosavuta komanso kukhala wotsika mtengo.

Mtsogoleri wa dziko lino, Dr Lazarus Chakwera, adanena pomwe ankatenga boma kuti adzaonetsetsa kuti maulendo apa njanji ayambirenso mdziko muno.

Masiku apitawa, sitima inayendanso kuchoka ku Blantyre kufika ku Lilongwe itanyamula malasha.

Print Friendly, PDF & Email

Author

  • Mayeso Chikhadzula joined MBC in 2006, he's an Investigative Journalist and Principal Reporter. He's also a News Anchor, Presenter, and producer.

Related posts

Malawi takes climate justice fight to ICJ

MBC Online

Chakwera ali pa mkumano ndi mabungwe othandiza pa ngozi zogwa mwadzidzidzi

Chimwemwe Milulu

Woman caught trying to sell own child

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.