Malawi Broadcasting Corporation
Agriculture Development Local Local News Nkhani

‘Osazembetsa thandizo la chimanga’

Wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino Dr Michael Usi wati ndi okhumudwa ndi mchitidwe wa anthu ena amene akumaba thandizo la chimanga lomwe Boma likupereka kwa omwe akhudzidwa ndi njala m’dziko muno.

Dr Usi ati achita chotheka kuti m’chitidwewu uthe. Iwo ati ena omwe akuulimbikitsa ndi adindo.

Iwo anena izi pamene amatsogolera ntchito yogawa chakudya mu mzinda wa Blantyre kwa anthu okhala mu Ward ya Soche East.

Pa mwambo wina ogawa chakudyachi omwe ukuchitikira mkati mwa bwalo la Kamuzu ku Blantyre, anthu ena anapezekanso akufuna kuzembetsa chimanga, koma anawalanda asanapite patali.

Masiku awiri apitawo, Dr Usi amatsogoleranso ntchito ngati yomweyi ku Chilomoni komwe anapezanso achinyamata ena akufuna kuzembetsa chimanga.

Related posts

TNM for partnerships that transform lives

Alinafe Mlamba

PRISAM condemns school vandalism, urges police to name and arrest culprits

McDonald Chiwayula

OLD MUTUAL AND WESM PARTNER TO RESTORE VEGETATION ON MICHIRU MOUNTAIN

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.