Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Politics

Mia wati adzapikisana nawo pampando wa wachiwiri kwa wachiwiri kwa mtsogoleri ku MCP

A Abida Sidik Mia omwe ndi nduna yaza madzi ndi ukhondo komanso phungu wadera la Chikwawa Mkombezi, anakaonekela ku ofesi yachigawo chapakati ya chipani cha Malawi Congress (MCP) komwe alengeza chidwi chawo kudzaimira pa udindo wa wachiwiri kwa wachiwiri wa mtsogoleri wa chipani cha MCP pa msonkhano waukulu wa konveshoni.

Poyankhula kwa amene anafika ku ofesiyi, a Mia ati ndi wokonzeka kudzapitiriza ntchito yolimbikitsa chipani cha MCP pokonzekera chisankho cha 2025.

M’mawu ake, wapampando wachipani cha MCP mchigawo chapakati a Patrick Zebron Chilondola ati ndi wokondwa kuti nao amayi muchipanichi ali ndi chidwi chokhala mmaundindo osiyanasiyana, zomwe Prezidenti wa dziko lino amalimbikitsa.

 

Print Friendly, PDF & Email

Author

  • Mayeso Chikhadzula joined MBC in 2006, he's an Investigative Journalist and Principal Reporter. He's also a News Anchor, Presenter, and producer.

Related posts

CHAKWERA ENGAGES SOUTHERN REGION CHIEFS IN DEVELOPMENT DIALOGUE

MBC Online

Chakwera departs Maputo for 44th SADC Heads of State Summit in Harare

Austin Kachipeya

SCTP boosts livelihoods in Nkhata Bay

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.