Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

‘Andale asamalowelere ntchito zam’ma khonsolo’

Boma lapempha anthu ochita ndale m’dziko muno kuti asamalowelere ntchito za ma khonsolo ndi cholinga chofuna ku kwaniritsa zolinga zawo pa ndale.

Nduna ya za maboma a ang’ono, a Richard Chimwendo Banda, ndi amene ananena izi mu mzinda wa Blantyre pamkumano wa masiku awiri womwe adindo a m’ma khonsolo a m’chigawo cha kumwera amafotokoza momwe agwilira ntchito zawo kwa miyezi ingapo yapitayo.

Ndunayi inapemphanso atsogoleri m’ma khonsolowo kuti azigwira ntchito zotumikira anthu omwe ndi osowa.

A Chimwendo Banda anatinso m’chitidwe wosokoneza ntchito za chitukuko m’ma khonsolo umakula maka pamene dziko likuyandikira kuchita chisankho.

“Musalole kuti ntchito zachitukuko ziime chifukwa chofuna kusangalatsa anthu ena a ndale, ” a Chimwendo Banda anatero.

Pamkumanowu, kunali a bwanankubwa, oyang’anira ntchito za chuma m’ma khonsolo, aphungu akunyumba yamalamulo komanso ma khansala a m’chigawo cha kum’mwera mwa ena.

Related posts

Madam Chakwera afika ku mwambo okumbukira tsiku la anthu achialubino

Rabson Kondowe

Awamanga ataba matumba 300 a chimanga cha ADMARC

Romeo Umali

MAIIC yapanga phindu lokwana K2.5 billion mu 2023

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.