Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani

Akatswiri amalamulo ati ulendo wa Kabambe ukadalipo

Akatswiri pa nkhani zamalamulo a Justin Dzonzi ndi a Allan Ntata ati ntchito ikadalipo kwa amene akutsogolera chipani cha UTM, a Dalitso Kabambe, pa nkhani yawo imene ili kubwalo lamilandu.

Izi zikudza pamene bwalo lamilandu lalikulu lakana pempho la a Kabambe kuti liyimitse mlandu owaganizira kuti adagwiritsa ntchito mopanda chilolezo komanso kubisa $350 million pamene iwo adali mkulu wa Reserve Bank.

A Henry Mathanga, Cliff Chiunda komanso a Joseph Mwanamveka akukhudzidwanso ndi nkhaniyi.

M’modzi wa akatswiri a za malamulo, a Dzonzi, anati nfundo zimene a Kabambe adapititsa kubwaloli sizinali zogwira mtima.

Iwo ati mlanduwu uyenera kupitirira potsatira magawo awiri motsatira umboni umene a mbali ya boma apereke bwaloli lisadapereke chiganizo chake ngati kudzakhale koyenera kuti mlanduwu upitirire kapena ayi.

Ndipo a Ntata anati udindo uli onse wa munthu yemwe akugwira ntchito zaboma supereka chitetezo choti sungayimbidwe mlandu uliwonse monga momwe amafunira a Kabambe.

Pakadali pano, mkulu wozenga milandu kumbali ya boma, a Masauko Chamkakala, anati mboni zawo zonse ndi zokonzeka pa nkhaniyi.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

CIVIL SOCIETY WEIGHS IN ON KAPONDAMGAGA’S REINSTATEMENT

MBC Online

Ayamikira Chitukuko cha milatho

MBC Online

Perekani mauthenga achisankho mosakondera – MEC

Simeon Boyce
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.