Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani

Akatswiri amalamulo ati ulendo wa Kabambe ukadalipo

Akatswiri pa nkhani zamalamulo a Justin Dzonzi ndi a Allan Ntata ati ntchito ikadalipo kwa amene akutsogolera chipani cha UTM, a Dalitso Kabambe, pa nkhani yawo imene ili kubwalo lamilandu.

Izi zikudza pamene bwalo lamilandu lalikulu lakana pempho la a Kabambe kuti liyimitse mlandu owaganizira kuti adagwiritsa ntchito mopanda chilolezo komanso kubisa $350 million pamene iwo adali mkulu wa Reserve Bank.

A Henry Mathanga, Cliff Chiunda komanso a Joseph Mwanamveka akukhudzidwanso ndi nkhaniyi.

M’modzi wa akatswiri a za malamulo, a Dzonzi, anati nfundo zimene a Kabambe adapititsa kubwaloli sizinali zogwira mtima.

Iwo ati mlanduwu uyenera kupitirira potsatira magawo awiri motsatira umboni umene a mbali ya boma apereke bwaloli lisadapereke chiganizo chake ngati kudzakhale koyenera kuti mlanduwu upitirire kapena ayi.

Ndipo a Ntata anati udindo uli onse wa munthu yemwe akugwira ntchito zaboma supereka chitetezo choti sungayimbidwe mlandu uliwonse monga momwe amafunira a Kabambe.

Pakadali pano, mkulu wozenga milandu kumbali ya boma, a Masauko Chamkakala, anati mboni zawo zonse ndi zokonzeka pa nkhaniyi.

Related posts

Budget presentation concluded

Romeo Umali

Dalitso Khungwa: immovable wall behind Wanderers’ unbeaten run

Rabson Kondowe

Communities urged to advocate for climate justice

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.