Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani

Akatswiri amalamulo ati ulendo wa Kabambe ukadalipo

Akatswiri pa nkhani zamalamulo a Justin Dzonzi ndi a Allan Ntata ati ntchito ikadalipo kwa amene akutsogolera chipani cha UTM, a Dalitso Kabambe, pa nkhani yawo imene ili kubwalo lamilandu.

Izi zikudza pamene bwalo lamilandu lalikulu lakana pempho la a Kabambe kuti liyimitse mlandu owaganizira kuti adagwiritsa ntchito mopanda chilolezo komanso kubisa $350 million pamene iwo adali mkulu wa Reserve Bank.

A Henry Mathanga, Cliff Chiunda komanso a Joseph Mwanamveka akukhudzidwanso ndi nkhaniyi.

M’modzi wa akatswiri a za malamulo, a Dzonzi, anati nfundo zimene a Kabambe adapititsa kubwaloli sizinali zogwira mtima.

Iwo ati mlanduwu uyenera kupitirira potsatira magawo awiri motsatira umboni umene a mbali ya boma apereke bwaloli lisadapereke chiganizo chake ngati kudzakhale koyenera kuti mlanduwu upitirire kapena ayi.

Ndipo a Ntata anati udindo uli onse wa munthu yemwe akugwira ntchito zaboma supereka chitetezo choti sungayimbidwe mlandu uliwonse monga momwe amafunira a Kabambe.

Pakadali pano, mkulu wozenga milandu kumbali ya boma, a Masauko Chamkakala, anati mboni zawo zonse ndi zokonzeka pa nkhaniyi.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Anglican Church offers free secondary education in BT

MBC Online

Dedza DEST urged to be professional ahead of 2025 polls

MBC Online

Centenary Bank partners with Tourism Ministry

Yamikani Simutowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.