Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani

Akatswiri amalamulo ati ulendo wa Kabambe ukadalipo

Akatswiri pa nkhani zamalamulo a Justin Dzonzi ndi a Allan Ntata ati ntchito ikadalipo kwa amene akutsogolera chipani cha UTM, a Dalitso Kabambe, pa nkhani yawo imene ili kubwalo lamilandu.

Izi zikudza pamene bwalo lamilandu lalikulu lakana pempho la a Kabambe kuti liyimitse mlandu owaganizira kuti adagwiritsa ntchito mopanda chilolezo komanso kubisa $350 million pamene iwo adali mkulu wa Reserve Bank.

A Henry Mathanga, Cliff Chiunda komanso a Joseph Mwanamveka akukhudzidwanso ndi nkhaniyi.

M’modzi wa akatswiri a za malamulo, a Dzonzi, anati nfundo zimene a Kabambe adapititsa kubwaloli sizinali zogwira mtima.

Iwo ati mlanduwu uyenera kupitirira potsatira magawo awiri motsatira umboni umene a mbali ya boma apereke bwaloli lisadapereke chiganizo chake ngati kudzakhale koyenera kuti mlanduwu upitirire kapena ayi.

Ndipo a Ntata anati udindo uli onse wa munthu yemwe akugwira ntchito zaboma supereka chitetezo choti sungayimbidwe mlandu uliwonse monga momwe amafunira a Kabambe.

Pakadali pano, mkulu wozenga milandu kumbali ya boma, a Masauko Chamkakala, anati mboni zawo zonse ndi zokonzeka pa nkhaniyi.

Related posts

YPES launches environmental website to promote sustainability

Romeo Umali

Human Trafficking persists

Romeo Umali

Former Flames goalie no more

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.