Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

‘Nsomba zipezeke komanso zotsika mtengo’

Nduna yoona za chilengedwe, a Michael Usi, yauza akuluakulu  osiyanasiyana ogwira ntchito za kafukufuku  zokhudza nsomba kuti agwiritse ukadaulo wawo ndi kuonetsetsa kuti achitapo kanthu poonjezera chiwerengero cha nsomba ndi kuonetsetsa kuti m’malawi aliyense akuzipeza pa mtengo otsika.

Ndunayi yanena izi ku Bingu International Convention Centre pa zokambirana zokhudza  mmene ndondomeko za nsomba zomwe anakhazikitsa zotchedwa National Plan of Action for Small Scale Fisheries zikuyenera kugwilira ntchito.

A Usi apemphanso a zakafukufukuwa kuti aonetsetse kuti zotsatira  zakafukufuku yemwe amachita  zikupezeka, akuzigawa komanso akuzigwiritsa ntchito kuti cholinga chake  chopindulira dziko lino chikwaniritsidwe.

Iwo ati kwa nthawi yaitali, dziko lino lakhala likungokamba ndi kuchita kafukufuku koma  osachitapo kanthu ndipo ati akufuna kuti akuluakuluwa achitepo kanthu kuti aMalawi apindule popeza nsombazi mosavuta komanso motsika mtengo.

Ndunayi yati ili  ndi chiyembekezo kuti zomwe atakambirane pa msonkhanowu zipereka mndandanda wa zomwe aliyense atachite  pokwaniritsa izi osati kungoyankhula chabe.

 

Related posts

Football management improves in Eastern Region

Romeo Umali

Martyrs’ Day commemoration service of worship underway

Rabson Kondowe

PMRA yatsutsa kuti m’dziko muno muli mankhwala ambiri osavomerezeka

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.