Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

PMRA yatsutsa kuti m’dziko muno muli mankhwala ambiri osavomerezeka

Bungwe la Pharmacy and Medicines Regulatory Authority (PMRA) latsutsa kafukufuku wa sukulu ya ukachenjede ya m’dziko la Ethiopia lomwe linati dziko la Malawi muli chiwerengero chachikulu cha mankhwala osavomerezeka komanso olowa mwa chinyengo mu Africa.

Mkulu wa bungweli, a Mphatso Kawaye, ati kafukufukuyi ndi wam’chaka cha 2015 ndipo sakuyimira mankhwala onse kaamba kakuti analunjika pa mankhwala a Malungo a mu zipatala zomwe sizaboma.

“Zitha kutheka kuti kasamalidwenso kamankhwalawa kanali kovuta kaamba koti zotsatira zamankhwala omwe anayeza zimasiyanasiyana ndipo ndizovuta kuzikhulupilira ,” anatero a Kawaye.

M’modzi mwa akulu ku unduna wazaumoyo, a Godfrey Kadewere, ati boma pamodzi ndi PMRA akuyesetsa powonetsetsa kuti mankhwala m’zipatala ndi ovomerezeka komanso sakupereka chiopsezo pa umoyo wa anthu.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

FIRST LADY IS TB CHAMPION

MBC Online

Chakwera to attend 79th UNGA session

MBC Online

CCAP Women guild taught to overcome iniquities

Sothini Ndazi
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.