Malawi Broadcasting Corporation
Entertainment Nkhani

Zonke wabweranso ndi nyimbo yatsopano

Mmodzi mwa oimba nyimbo za achinyamata, Zonke Too Fresh, watulutsa kanema wa nyimbo yake yatsopano yotchedwa Vote.

Mu nyimboyi, Zonke Too Fresh, yemwe dzina lake leni leni ndi Zaithwa Mhone, akumemeza ngenge ( chiphadzuwa) kuti isankhe iye monga muja andale achitira pokopa anthu.

“Mphoto yomwe a Malawi anandipatsa kudzera mu MBC Entertainers of Year inandipatsa nyonga zapadera kuti ndipitirize kutulusa nyimbo zabwino,” watero Zonke.

Zonke Too Fresh, yemwe ali ndi zaka 22, ndiyemwe akusunga mphoto ya kanema wapamwamba mu MBC Entertainers of Year ndi nyimbo yake ya Kambuzi.

Iye amadziwikanso ndi nyimbo monga school report, pachibale pawo, mankhwala ndi mkazi wa mkalasi.

Related posts

Lucius anali katswiri, watero ‘Reggae Ambassador’ Charles Sinetre

Romeo Umali

Malawian Artists set to shine at Jamaica’s Reggae Month

MBC Online

Dekhani AMalawi zikutheka — Chakwera

Mayeso Chikhadzula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.