Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

UTM yalimbikitsa achinyamata

Chipani cha UTM chalimbikitsa achinyamata kuti alembetse mu kaundula wa unzika kuti adzakhale ndi mwai oponya nawo voti  pachisankho chachikulu chomwe chichitike mdziko muno chaka cha mawa.

Mkulu wa achinyamata mu chipanichi a Penjani Kalua amalankhula izi ku Mangochi pa mwambo okweza mbendera ya chipanichi.

Chipani cha UTM akuti chinatsitsa mbendera yake mwezi wa June potsatira imfa ya mtsogoleri wake yemwenso anali wachiwiri kwa mtsogoleri wadziko lino, Dr Saulos Chilima.

“Tikupempha achinyamata onse omwe akufuna kudzaponya nawo voti  kuti asachite ulesi olembetsa mkaundula wa chiphaso cha unzika ngati akufuna kudzaponya nawo voti mwezi wa September chaka cha mawa,” anatero a Kalua.

 

Olemba: Owen Mavula

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Chipatala cha South Lunzu chikupempha thandizo

Simeon Boyce

WORLEC calls for equality, inclusivity for women in politics

MBC Online

Mwakifwamba Youth Club advocates for a clean environment

Rudovicko Nyirenda
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.