Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

UTM yalimbikitsa achinyamata

Chipani cha UTM chalimbikitsa achinyamata kuti alembetse mu kaundula wa unzika kuti adzakhale ndi mwai oponya nawo voti  pachisankho chachikulu chomwe chichitike mdziko muno chaka cha mawa.

Mkulu wa achinyamata mu chipanichi a Penjani Kalua amalankhula izi ku Mangochi pa mwambo okweza mbendera ya chipanichi.

Chipani cha UTM akuti chinatsitsa mbendera yake mwezi wa June potsatira imfa ya mtsogoleri wake yemwenso anali wachiwiri kwa mtsogoleri wadziko lino, Dr Saulos Chilima.

“Tikupempha achinyamata onse omwe akufuna kudzaponya nawo voti  kuti asachite ulesi olembetsa mkaundula wa chiphaso cha unzika ngati akufuna kudzaponya nawo voti mwezi wa September chaka cha mawa,” anatero a Kalua.

 

Olemba: Owen Mavula

Related posts

Student hopes to excel in English at regional Spelling Bee contest

Romeo Umali

Three Wanderers players nominated for Castel Award

Romeo Umali

JTI re-launches tobacco farmers incentive programme

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.