Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News Nkhani Politics

TIGWIRANE MANJA NDI BOMA PA CHITUKUKO -MATOLA

Nduna yoona zamphamvu zamagetsi a Ibrahim Matola yati nkofunika kuti anthu onse m’dziko muno agwirane manja popititsa patsogolo chitukuko mogwirizana ndi masomphenya a mtsogoleri wa dziko lino Dr Lazarus Chakwera.

A Matola ayankhula izi m’boma la Balaka komwe amakumana ndi mamembala azipani zosiyanasiyana zomwe zili mumgwilizano wa Tonse komanso ochita malonda.

Malinga ndi a Matola cholinga cha msonkhanowu ndi mamembala a People’s Party (PP) komanso a UTM kunali kufuna kuwafotokozela kuti amvetse bwino zomwe Dr Chakwera anayankhula m’nyumba ya malamulo potsekulira msonkhano wa aphungu.

Mwa zina a Matola anatsimikiza kuti ndi utsogoleri wa Dr Chakwera, aonetsetsa kuti vuto lakuthimathima kwa magetsi lithe ncholinga choti ntchito zamalonda zipite patsogolo.

M’mau ake mkulu wa anthu a bizinesi m’boma la Balaka, a William Kasonda, wapempha kuti ngongole za NEEF ziwafikire.

Olemba Mayeso Chikhadzula.

#mbconlineservices

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Chakwera to attend World Bank summit in Kenya

MBC Online

MALAWI TO BENEFIT FROM UNCTAD  PRODUCTIVE CAPACITIES INITIATIVE

McDonald Chiwayula

GIRL ENDS LIFE AFTER DISPUTE WITH FATHER

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.