Malawi Broadcasting Corporation
Business Development Local Local News

Salima Sugar iphunzitsa adindo awo utsogoleri

Salima Sugar yati yayamba kuphunzitsa maphunziro a utsogoleri kwa anthu omwe ali ndi udindo pa kampani yawo pofuna kupititsa ntchito patsogolo.

Wapampando wa kampaniyi, a Wester Kosamu, ati zaka za m’mbuyomu pa kampaniyi pakhala pali chipwirikiti pa ntchito chifukwa ati akhala akuyendetsedwa ndi anthu ena oti analibe ukadaulo komanso mapepala owayenereza.

A Kosamu ati kupatula kusula adindowa ndikuwatumiza ku sukulu za ukachenjede, akhazikitsanso mulozo watsopano oyendetsera kampaniyi kuti izipanga phindu lochuluka ndikuonesetsa kuti Sugar wake akupezeka pa msika mosavuta komanso okwanira.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Youths tipped to think big

MBC Online

Mtsikana wa zaka 17 wapha mwana

Romeo Umali

Malawi, Botswana strengthen ties

Paul Mlowoka
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.