Malawi Broadcasting Corporation
Business Development Local Local News

Salima Sugar iphunzitsa adindo awo utsogoleri

Salima Sugar yati yayamba kuphunzitsa maphunziro a utsogoleri kwa anthu omwe ali ndi udindo pa kampani yawo pofuna kupititsa ntchito patsogolo.

Wapampando wa kampaniyi, a Wester Kosamu, ati zaka za m’mbuyomu pa kampaniyi pakhala pali chipwirikiti pa ntchito chifukwa ati akhala akuyendetsedwa ndi anthu ena oti analibe ukadaulo komanso mapepala owayenereza.

A Kosamu ati kupatula kusula adindowa ndikuwatumiza ku sukulu za ukachenjede, akhazikitsanso mulozo watsopano oyendetsera kampaniyi kuti izipanga phindu lochuluka ndikuonesetsa kuti Sugar wake akupezeka pa msika mosavuta komanso okwanira.

 

Related posts

MCC 2nd Compact to impact millions of Malawians-Chakwera

Romeo Umali

INFRASTRUCTURE DEVELOPMENT CRUCIAL FOR TRADE DEVELOPMENT IN AFRICA – CHAKWERA

Blessings Kanache

Farmers in Chiradzulu embrace commercialisation drive

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.