Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Osagulitsa ndi kugula chiponde – Unduna wazaumoyo

Unduna wazaumoyo wachenjeza anthu kuti asiye mchitidwe ogulitsa ndi kugula chiponde kapena kuti “Ready to Use Therapeutic Food” mu chingerezi.

Malinga ndi chikalata chomwe undunawu watulusa ndipo wasainira ndi mlembi wamkulu muundunawu, a Samson Mdolo, mchitidwewu ukukolezera kusowa kwa chiponde muzipatala zaboma.

Azaumoyo amapereka chiponde maka kwa anthu omwe ali onyetchera.

A Mdolo ati mchitidwewu ukuchitika ngakhale pamapaketi a chipondechi analemba kuti sichogulitsa, ndipo izi zithanso kudzetsa mavuto ena kwa anthu omwe akumadya opanda uphungu wa akatswiri azachipatala.

Pamenepa, iwo amemeza anthu m’dziko muno kuti adzikaneneza kupolisi anthu omwe akugulisa chiponde mosatsata malamulo.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Musadalire kusewera ndi m’khala kale — Mapopa

Romeo Umali

Pezani nkhani za MBC pa WhatsApp kapena SMS

MBC Online

Tisagulise chimanga chathu chidakali kumunda —Makwangwala

Timothy Kateta
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.