Malawi Broadcasting Corporation
Development Local News Nkhani

NRB yalemba anthu opitilira 1.5 miliyoni mu ndondomeko yakalembera

Bungwe la National Registration Bureau lati lalemba anthu 1,556,613 pa ndondomeko ya kalembera ya chiphaso cha unzika.

Mlembi wamkulu wa bungwe la National Registration Bureau, Mphatso Sambo, wati chiwerengerochi n’chachikulu poyerekeza ndi chiwerengero cha anthu 1,500,000 omwe amafuna kulembetsa.

Sambo wati bungwe lawo liyambanso kalembera wina pa 10 mwezi uno ndipo afikira madera onse adziko lino muma centre 5002, poyerekeza ndi ma centre 1250 omwe adafikira poyamba.

Sambo waonjezeranso kuti bungwe la NRB lakweza chiwerengero chosindikiza ziphaso za unzika ndipo pano akusindikiza ziphaso 15,000 pa tsiku.

 

Related posts

Dr Chakwera returns on Saturday

Romeo Umali

First Lady’s Shaping the Future Foundation Hosts Fundraising Dinner at Kamuzu Palace

Alinafe Mlamba

Anthu akukhamukira kumwambo wa Chikumbutso ku Mulanje

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.