Malawi Broadcasting Corporation
News Nkhani

Ndende si malo okhaulitsa anthu – Wisikoti

Mkulu oyang’anira ndende za m’dziko muno, a Masauko Ng’ombeyagwada Wisikoti, ati kundende ndi malo othandiza kusintha khalidwe la munthu osati malo ongokhaulitsira iwo ophwanya malamulo.

A Wisikoti amafotokoza izi pamene bungwe la Uthunthu limakhazikitsa m’gwirizano ndi bungwe la TEVETA kuti lidziphunzitsa achinyamata a ndende za m’dziko muno maphunziro ambiri kuti akadzakhala mfulu asadzasowe poyambira.

Bungwe la Uthunthu ndi la chikhristu ndipo limathandiza anthu kukhala odzidalira paokha kudzera m’maphunziro a ntchito zamanja.

Mkulu wa bungweli, a Caswel Mkanda, ati agwiritsa ndalama zokwana K100 million zomwe anasonkha ndi mamembala awo ndipo anamema anthu akufuna kwabwino kuti awathandize kupitiliza zimene ayambazi.

Poyankhulapo, mkulu wa bungwe la TEVETA, a Elwin Chiwembu-Sichiola, ati maphunziro amenewa akayambira ku ndende za Maula ndi Kachere mu Mzinda wa Lilongwe.

A Sichiola ayamikira bungwe la Uthunthu ndipo ati apitiliza kugwira nalo ntchito limodzi.

Related posts

Chinese EV manufacturer targets Zimbabwe, Malawi in Africa expansion drive

MBC Online

Partners in Hope opens dialysis and ICU units for improved healthcare

Rabson Kondowe

Reaping from Young Builders Challenge

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.