Malawi Broadcasting Corporation
Uncategorized

Mwaungulu ndi Kumwenda awayambitsa lero

Mphunzitsi wa timu ya Flames Patrick Mabedi wasintha malo awosewera awiri mtsiku la lero kusiyana ndi timu yomwe inayamba m’masewero apa bwalo la Bingu ndi timu ya Sao Tome sabata yatha.

Mabedi wakhulupilira ntchito za Patrick Mwaungulu ndi Henri Kumwenda omwe anachita kuchokera panja m’masewero apita.

Masanawa Flames yomwe ili ndi mapointi asanu ndi imodzi ikumana ndi Equatorial Guinea yomwe ilibe pointi ngakhale imodzi atawachotsera mapointi onse kaamba koseweretsa munthu yemwe sanali woyenera kusewera.

Flames ili panambala yachinayi pomwe Equatorial Guinea ndiyachisanu mugululi.

Related posts

MOZAMBICAN WINS CHAKWERA PUBLIC SPEAKING PRIZE

Mayeso Chikhadzula

Activists want sanitary pads accessible for free

Alinafe Mlamba

Irrigation key to food security, farmers appeal for assistance

Steve Dakalira
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.