Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Religion

‘Musalole andale kukutumani kuti muchite ziwawa’

Achinyamata awalangiza kuti asaononge tsogolo lawo polola kuti andale adziwagwiritsa ntchito yoyambitsa ziwawa pamene dziko lino likukonzekera chisankho m’mwezi wa September chaka chino.

M’busa Chipasi Chirwa ndiye wapereka langizoli mu ulaliki wake pa mpingo wa St Andrews CCAP munzinda wa Mzuzu.

“Kukhala membala wachipani chilichonse sikolakwika, mukhoza kukachita chi khristu ku chipani komweko posakalola kugwiritsidwa ntchito yochita ziwawa,” M’busa Chirwa anatero.

Iwo analangiza achinyamata kuti azindikire kuti andale amene amawatuma ndi akuluakulu kale komanso kwawo kwatsala kochepa.

Abusawa analangizanso akhristu kuti adzipereka msonkho ku boma moyenera monga momwe mawu a Mulungu amanenera kuti “perekani kwa Kaisara zake za Kaisara” m’bukhu la Maliko ndime 12 vesi ya 17.

M’busa Chirwa anati akhristu akuyenera kukhala okhulupirika ndi kuti kaya ali mumsika adzipereka msonkho wamumsikawo komanso ngati ali ndi ntchito zamalonda akuyenera kulipira moyenera

Olemba: Henry Haukeya

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

“A Gotani – Hara ali ndi luntha potsogolera” — President Chakwera

Timothy Kateta

Jiya wayamikira chitukuko, wadzudzula mchitidwe oononga

MBC Online

All set for Science for All national quiz

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.