Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News Nkhani Politics

Msonkhano waukulu tichita mu September — JB

Prezidenti wa chipani Cha PP, Dr Joyce Banda walengeza kuti chipanichi chidzakhala ndi msonkhano wake waukulu pa 7 September chaka chino mumzinda wa Lilongwe.

Iwo alengeza izi ku Nancholi komwe anachititsa msonkhano wandale.

Iwo ati ndi okondwa kuti chipani cha PP ndi champhamvu ku Blantyre ndipo apempha owatsatira kuti apitirize kusunga bata.

Khwimbi la anthu linasonkhana kumsonkhanowu pabwalo la Nancholi ndipo nawo aGeorge Nnesa, mtsogoleri wa chipani Cha Mafunde, analinso nawo pa msonkhanowu.

Olemba: Blessings Cheleuka
#MBCDigital
#Manthu

Related posts

Tipitiliza kulumikizitsa anthu omwe anathawa kwawo – MRCS

Rabson Kondowe

Youths urged to boost development through innovation

Rabson Kondowe

Boma likufuna kutukula ulimi wa thonje — Kawale

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.