Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

MACRA ikufuna mtengo wa ‘smartphone’ utsike

Bungwe la Malawi Communications Regulatory Authority (MACRA) lati likufuna mitengo ya ma ‘smartphone’ kapena kuti lamya zammanja zomwe  ziri ndi  ‘internet’ zikhale zotsika mtengo mdziko muno.

Mkulu wa bungweli a Daud Suleman wati kukwera mtengo kwa lamya zammanjazi  kukuchititsa kuti a Malawi ochepa okwana 1 million okha akhale ndi mwayi ogwiritsa ntchito zinthu zomwe zikupezeka pa makina atsopano a ‘internet’.

Apa iwo ati kukwera mtengoku kukuchitika chifukwa choti lamyazi amachita kuyitanitsa kuchokera mayiko akunja ndikuti zikamafika kuno zimakwera mtengo kwambiri.

“Poyesetsa kuti lamyazi zitsike mtengo tili ndi chikonzero chothandizana ndi makampani ena kuti tidziyitanitsa zipangizo zopangira malamyawa kuti tidzilumikiza konkuno ndicholinga choti mitengo itsike,” anatero a Suleman.

 

Wolemba: Henry Haukeya

Related posts

Roads Authority impressed with M1 rehabilitation progress

Mayeso Chikhadzula

Osagwiritsa ntchito imfa ya Chilima pa ndale

Rabson Kondowe

‘Adolescents should have access to sexual and reproductive health services’

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.