Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Sports Sports

Ellen Simwaka akufuna lamba wa WBC

Katakwe otchaya nkhonya, Ellen Simwaka, wati wayika chidwi chofuna kutenga lamba wa World Boxing Council (WBC) akapatsidwa mpata okumana ndi amene akufunanso lambayu.

Simwaka wayankhula izi pamene wabweleranso mu ring ndi chipambano atagonjetsa Jesca Mfinanga, wa m’dziko la Tanzania, kudzera pa ma points mu nkhonya imene inalipo usiku wapitawu ku Tanzania.

Osewerayu, amene amakhala m’dziko la South Africa, anati akumasowa masewero chifukwa osewera ena akumamuopa ndi kumukana kuti asewere naye.

“Yemwe ankasunga lambayu, Kudakwache Chiwandire, wa ku Zimbabwe adakana kusewera nane nkhonya yokonzakonza patangotsala masiku ochepa,” anadandaula Simwaka.

Padakalipano, katakwe pa zigogodoyu akusungira malamba akuluakulu awiri a WBF komanso International Boxing Federation komanso iye ali pa nambala yoyamba mu Africa mu gulu la Bantam Weight.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Osewera mpira wa asungwana akusokonekera

MBC Online

Suicide Cases worry Neno Police

Romeo Umali

CHAKWERA URGES DIASPORA MALAWIANS TO INVEST BACK HOME

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.