Malawi Broadcasting Corporation
Development Local News Nkhani

Dr Chilima afika m’dziko la Korea

Wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino Dr Saulos Chilima tsopano wafika m’dziko la Republic of Korea kumene akachite nawo msonkhano waukulu pakati pa dzikolo ndi maiko amu Africa.

Nduna yoona za ulimi, a Sam Kawale, wachiwiri kwa mlembi ku ofesi ya mtsogoleri wa dziko lino, Dr Janet Banda SC, ndi ena mwa adindo akuluakulu a boma ndi amene analindira a Chilima pamodzi ndi akazi awo a Mary Chilima pa bwalo la ndege la Incheon.

Dr Chilima akuyimira m’tsogoleri wa dziko lino, Dr Lazarus Chakwera, pa msonkhanowu omwe ukhale ukuchitika koyamba m’dziko la Korea ndipo dziko lino lili pamodzi ndi maiko makumi asanu ndi mphambu zinayi (54) amene ndi ochokera ku Africa.

Imodzi mwa nkhani zikuluzikulu zomwe zimange nthenje ku mkumanowu ndi yokhudzana ndi kulimbikitsa ntchito zamalonda pakati pa dziko la Korea ndi maiko a mu Africa.

Olemba: Timothy Kateta, Seoul, Republic of Korea

Related posts

Malawi to conduct trials on new TB vaccine

Romeo Umali

Local entertainers should strive for global collaborations – Multichoice

Rabson Kondowe

Bandera ali mchitokosi pomuganizira kuti anazembetsa mtsikana wachichepere

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.