Malawi Broadcasting Corporation
Agriculture Development Local Local News Nkhani

Bungwe la FAO lithandiza dziko la Malawi

Bungwe loona zachakudya padziko lonse la FAO lati lipitiriza kugwila ntchito ndi dziko la Malawi powonetsetsa kuti boma likwaniritse masomphenya ake owonetsetsa kuti anthu ali ndi chakudya chokwanira.

Mkulu wa bungweli Qu Dongyu wanena izi atachita zokambirana ndi Prezidenti Dr Lazarus Chakwera ku likulu la bungweli ku Rome mdziko la Italy.

Mmau ake, Dr Chakwera anati boma lake likutsata mfundo zolimbikitsa ulimi, zokopa alendo komanso zamigodi pofuna kukweza dziko ndi miyoyo ya a Malawi.

Iwo anati anthu pafupifupi 5.5 million akufunika thandizo la chakudya mdziko la Malawi kaamba ka ng’amba yomwe inagwa m’maboma ambiri.

Pa chifukwachi a Dongyu ati agwira ntchito ndi boma la Malawi pothandiza anthu omwe akuvutika.

 

Related posts

LET’S NOT SQUANDER THIS OPPORTUNITY- USI TELLS UN CLIMATE CONFERENCE

MBC Online

ACTIONAID SET TO LAUNCH CLIMATE JUSTICE CAMPAIGN

McDonald Chiwayula

Judge for collective effort in promoting Human Rights, access to justice

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.