Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Local News Nkhani

Asilikali agwira nzika 276 zozembetsedwa zaku Ethiopia

Asilikali a Malawi Defence Force agwira nzika za dziko la Ethiopia 276, za zaka za pakati pa 15 ndi 40, zimene zinazembetsedwa kuchokera m’dziko lakwawo ndipo amazisunga ku malo okhala anthu othawa kwawo ku Dzaleka m’boma la Dowa.

Asilikaliwa agwiranso atsogoleri a mchitidwe ozembetsa anthuwu asanu ndi atatu amene ndi nzikanso za dzikolo ndipo amakhala ku Dzaleka komweko.

Iwo ati mchitidwewu ndi opereka chiwopsezo ku chitetezo cha dziko lino ngakhalenso kubweretsa matenda, mwazina.

Miyezi iwiri yapitayo, asilikaliwa anagwiranso anthu ena ozembetsedwa pafupifupi 250.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

NGORA urges NGOs to develop strategic plans

MBC Online

Driemo roped in for Chitipa United dinner and dance

Yamikani Simutowe

Another big winner!

Arthur Chokhotho
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.