Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Local News Nkhani

Asilikali agwira nzika 276 zozembetsedwa zaku Ethiopia

Asilikali a Malawi Defence Force agwira nzika za dziko la Ethiopia 276, za zaka za pakati pa 15 ndi 40, zimene zinazembetsedwa kuchokera m’dziko lakwawo ndipo amazisunga ku malo okhala anthu othawa kwawo ku Dzaleka m’boma la Dowa.

Asilikaliwa agwiranso atsogoleri a mchitidwe ozembetsa anthuwu asanu ndi atatu amene ndi nzikanso za dzikolo ndipo amakhala ku Dzaleka komweko.

Iwo ati mchitidwewu ndi opereka chiwopsezo ku chitetezo cha dziko lino ngakhalenso kubweretsa matenda, mwazina.

Miyezi iwiri yapitayo, asilikaliwa anagwiranso anthu ena ozembetsedwa pafupifupi 250.

 

Related posts

CARD touts success stories of the JOA projects

MBC Online

JENDA POLICE BUST 98 ILLEGAL IMMIGRANTS

McDonald Chiwayula

Countries urged to promote youth participation in politics

Alinafe Mlamba
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.