Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Local News Nkhani

Apolisi ku Mangochi amanga Boika atam’peza ndi chida choopsya

Apolisi ku Mangochi amanga a Boika Sabiti, 48, atawapeza ndi chida choopsya chopangidwa ndi zitsulo zosongoka komanso zokuthwa.

Ofalitsa Nkhani pa Polisi ya Mangochi, a Amina Tepani Daudi, ati a Sabiti adawapeza ndi chidachi pa malo omwela mowa m’boma la Mangochi.

“Tinawuzidwa ndi anthu ena akufuna kwabwino kuti a Sabiti akuyenda ndi chida choopsa chomwe anasunga m’chikwama chomwe amayenda nacho, ndipo ife apolisi tidathamangira kwa Mtalimanja komwe tinawapeza nacho,” a Daudi anatero.

Sabiti, amene amachokera m’mudzi wa Mapira ku Mangochi, ndi kabwerebwere kundende ndipo akaonekela kukhothi kukayankha mulandu opezeka ndi chida chowopsa.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Financial institutions urge construction players to explore funding opportunities

MBC Online

Mnyamata wamangidwa atabaya bwenzi lake

Davie Umar

“Tidzikondana tili moyo”

Mayeso Chikhadzula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.