Apolisi ku Mangochi amanga a Boika Sabiti, 48, atawapeza ndi chida choopsya chopangidwa ndi zitsulo zosongoka komanso zokuthwa.
Ofalitsa Nkhani pa Polisi ya Mangochi, a Amina Tepani Daudi, ati a Sabiti adawapeza ndi chidachi pa malo omwela mowa m’boma la Mangochi.
“Tinawuzidwa ndi anthu ena akufuna kwabwino kuti a Sabiti akuyenda ndi chida choopsa chomwe anasunga m’chikwama chomwe amayenda nacho, ndipo ife apolisi tidathamangira kwa Mtalimanja komwe tinawapeza nacho,” a Daudi anatero.
Sabiti, amene amachokera m’mudzi wa Mapira ku Mangochi, ndi kabwerebwere kundende ndipo akaonekela kukhothi kukayankha mulandu opezeka ndi chida chowopsa.