Malawi Broadcasting Corporation
Business Crime Local Local News Nkhani

Apolisi amanga msodzi yemwe anakhapa munthu pofuna kukhwima

Apolisi kwa Namalaka m’boma la Mangochi amanga Mofolo Yohane,22, yemwe ndi msodzi pomuganizira kuti anakhapa m’mutu Bashir Haji, wa zaka 13, ndi cholinga chakuti amuphe ndi kukhwimira malonda ake ogulitsa nsomba.

Ofalitsa nkhani za Polisi ya Mangochi, a Amina Tepani Daudi, atsimikiza nkhaniyi ndipo ati Mofolo akaonekera ku bwalo lamilandu kukayankha mulandu ofuna kupha.

“Titamufunsa Mofolo ananena kuti anawuzidwa ndi sing’anga kuti apititse zikope za munthu wakufa komanso madzi osambitsira maliro kuti bizinezi yake ipite patsogolo,” a Daudi anatero.

Yohane amachokera m’mudzi mwa William kwa mfumu yaikulu Nankumba ku Mangochi.

 

Related posts

UNDULE PREACHES HOPE FOR MALAWI’S ECONOMIC RECOVERY

Blessings Kanache

Teams, analysts weigh in on football calendar change

Romeo Umali

Let’s pray for one another — Usi

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.