Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Apolisi amanga anthu 696

Apolisi amanga anthu okwana 696 omwe akuwaganizira kuti apalamula milandu yosiyanasiyana mdziko muno.

Malinga ndi mneneri wa  apolisi mdziko muno a Peter Kalaya, ntchitoyi aigwira masiku atatu kuyambira lachitatu sabata yatha.

A Kalaya atinso apeza katundu osiyanasiyana yemwe akumuganizira kuti ndiobedwa.

Katunduyu ndi monga galimoto ziwiri, zipangizo za magalimoto, mankhwala a mchipatala kudzanso zakudya zosavomerezeka ndi zina zambiri.

Malinga ndi a Kalaya, ntchitoyi yomwe aigwira ndi maiko monga Zimbabwe, South Africa, Zambia, Angola ndi ena,  zithandiza kulimbikitsa maubale a kagwiridwe ka ntchito kabwino kudzanso kukhwimitsa chitetezo mu Africa.

 

Olemba : Ghwabupi Mwabungulu

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

SULOM charges MAFCO for Misconduct

MBC Online

Azimayi sakugwiritsa ntchito makondomu achizimayi

Simeon Boyce

GWENGWE CARRIES THE DAY

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.