Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News Nkhani

Anthu akusonkhana ku nyumba ya siwa kwa Dr Chilima

Anthu osiyanasiyana ayamba kufika kunyumba ya wachiwiri kwa mtsogoleri wadziko lino, Malemu Dr Saulos Chilima, ku Area 12 munzinda wa Lilongwe.

Ena mwa anthuwa ndi a Michael Usi omwe ndi wachiwiri kwa mtsogoleri wa chipani cha UTM komanso nduna yaza chilengedwe, mamembala a chipanichi, chomwe a Chilima anali mtsogoleri wake.

Mwambo onse wa maliro ukuyembekezeka kuchitikira kunyumba yawo yaboma ku Area 12.

Ndege yomwe Dr Chilima anakwera, pamodzi ndi anthu ena asanu ndi anayi, yapezeka itagwa mu nkhalango ya Chikangawa ndipo palibe amene wapulumuka pangoziyo.

 

Related posts

Apolisi agwira mbala zomwe zinaba katundu wa Radio Maria

Mayeso Chikhadzula

Four die in Lingadzi road accident

Romeo Umali

GOVT LAUDS MARANATHA ACADEMY

McDonald Chiwayula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.