Malawi Broadcasting Corporation
Local

ALIMI A MTEDZA APINDULA

Kampani yolimbikitsa ulimi ya Pyxus International yati ifikila alimi ochuluka ndi luso lamakono lomwe lithandize kuti mtedza olimidwa mdziko muno ukhale ovomerezeka ku misika ya pa dziko lonse.

Mkulu wa kampaniyi a Peiter Sikkel anena izi atakumana ndi mtsogoleri wa dziko la Malawi, Dr Lazarus Chakwera, pambali pa mnsonkhano wa bungwe la United Nations omwe ukuchitikira mu mzinda wa New York, m’dziko la America.

Iwo ati kampani yawo yakonzeka kuthandiza alimiwa ndi mbewu ya mtedza komanso kuwapezera misika yakunja.

Kampani ya Pyxus Agriculture Limited Malawi, ikugwila kale ntchitoyi ndi ndalama zochokera ku USAID komwe alimi ayamba kale kupindula.

 

#mbcmw
#mbcnewslive
#mbconlineservices

Related posts

NLGFC calls for smarter revenue models

Romeo Umali

Building cordial relationships pivotal for police effectiveness

Secret Segula

Improved Infrastructure, meals boost school enrolment in Malawi

McDonald Chiwayula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.