Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Akatswiri ovina nyimbo za soja akhetsa misozi

Akatswiri ovina nyimbo za Lucius Banda, Oliva Akimu komanso Isaac Nuru ati ndi osweka kamba ka imfa ya soja yemwe anali mzati pa moyo ndi luso lawo.

Poyankhula ndi MBC Digital, a Akimu ati a Banda ndi omwe anawatola ndikuwabweretsa poyera komanso kuthandizira kuti apeze maziko.

A Nuru ati anthu aphunzire kudzichepetsa monga Lucius Banda amachitira maka pothandiza kusula luso la ena.

“Apapa tikuthamangira ku Balaka kuti tikaperezeke bambo wathu Soja,” anatero onse awiri mosisima.

A Akimu ndi a Nuru akhala akuvina nyimbo za Lucius Banda kwazaka zoposa 20.

 

Related posts

Blue Eagles targets K13 million at fundraising dinner

Yamikani Simtowe

NAM launches fundraising for Junior Queens’ World Cup participation

Romeo Umali

Airtel partners Nokia to build terrestrial fiber network

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.