Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Adzudzula mmodzi mwa atsogoleri a DPP kaamba kolankhula moopseza

Bungwe la Civil Society Elections Integrity Forum ladzudzula mmodzi mwa atsogoleri a chipani cha Democratic Progressive (DPP) a Norman Chisale kaamba ka mchitidwe olankhula mau owoopseza komanso aukali pomwe akupangitsa misonkhano.

Mkulu wa bungweli a Benedicto Kondowe ati malankhulidwe woterewa akhoza kudzagwetsa mphwayi anthu omwe akufuna kudzaponya voti pachisankho chomwe chichitike pa 16 September chaka chino.

A Kondowe anatinso powonjezera kudzetsa mantha, izi zikhoza kudzabweretsa ziwawa.

Mwazina, a Chisale, omwe ndi mkulu owona za achinyamata mchipani cha DPP, akhala akumayankhula kuti mukuona kwawo,mavoti akhoza kudzaberedwa ndipo nawonso ali ndikuthekera kobera chisankho.

Iwo akhalanso akutchula atsogoleri ena andale maina monga a Khakhakha pongotchulapo ena.

Pakadali pano, mneneri wachipani cha DPP a Shadreck Namalomba ati malankhulidwe oterewa samayimira chipani chawo kotero izi ndi zosavomerezeka konse.

A Namalomba anawonjezeranso kunena kuti atsogoleri onse andale ayenera kupewa kulankhula mawu onyoza komanso oopseza ndipo mmalo mwake ayenera kufotokoza mfundo zomwe zikhonza kukopa anthu.

 

Olemba: Timothy Kateta

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Private sector mourns Dr Chilima

Justin Mkweu

A Chakwera alibe tsankho — Chimwendo Banda

Mayeso Chikhadzula

KATSONGA WOOS INDIAN INVESTORS

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.