Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Abusa asiye kudalira nkhosa zawo pachuma

Kampani ya Synthesis Agriculture yalangiza  abusa ena kuti asiye kudalira nkhosa zawo pa umoyo wawo wa tsiku ndi tsiku ndipo m’malo mwake ayambe kugwira ntchito zaulimi kuti azidzithandiza okha.

M’modzi mwa akuluakulu ku kampaniyi a Aaron Chitimbe wati nthawi yakwana  yoti abusa ayambe kudzidalira  pachuma.

Iwo ati pamene abusa akuwuza anthu kuti adzapita kumwamba akuyenera kudziwanso kuti asananyamuke ulendo wakumwamba akuyenera kuti akhale ndi chakudya padziko lapansi  pompano.

A Chitimbe alankhula izi pamaphunziro omwe cholinga chake ndikulimbikitsa abusa ubwino wochita ulimi pamene akukonzekera kupuma pantchito omwe akuchitikira mu mzinda wa Blantyre.

Maphunzirowa abweretsa pamodzi atumiki a Mulungu ochokera m’maboma osiyanasiyana chigawo cha kum’mwera.

Related posts

Youths lead in Malawi’s green business incentive project

Romeo Umali

Kakhobwe for sustainable reforestation

Romeo Umali

Stakeholders bang heads on tobacco smoke control

Yamikani Simtowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.