Malawi Broadcasting Corporation
Uncategorized

A Mutharika awunike zaka zawo asanaime – Mwakasungula

Katswiri pankhani zandale, a Undule Mwakasungula, wapempha mtsogoleri wakale wa dziko lino Professor Peter Mutharika kuti awunike mozama za zaka zawo ngati angadzakwanitse kutsogolera dziko lino moyenera.

Mu kalata yomwe a Mwakasungula atulutsa, iwo ati a Mutharika atsogoze kukonda dziko lino ndipo avomereze kuti pali zinthu zambiri zomwe boma la Tonse lakwanitsa kuzikonzanso ndikuchita potukula dziko lino.

Iwo ati potengera zaka zakubadwa, ndi zokaikitsa ngati a Mutharika angakwanitse kuyendetsa dziko lino mosadodoma.

Wolemba: Blessings Cheleuka

Related posts

LOWER SHIRE FACES FLOODS THREAT

MBC Online

CHAKWERA HAILS CULTURE AS PANACEA FOR UNITY

MBC Online

BWB secures $145 million for operational improvements

Alinafe Mlamba
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.