Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

A Malawi Mudzifunsa Mafunso Atsogoleri Anu Mmalo Momangodandaula — Usi

Nduna yoona za chilengedwe ndi kusintha kwa nyengo, Dr Michael Usi, yalangiza a Malawi kuti adzitha kumafunsa mafunso  atsogoleri awo mmalo momangodandaula akaona kuti zinthu sizikuyenda moyenera.

https://youtu.be/GXBmM9R_U7E

A Usi amayankhula ku Chirimba CCAP mu mzinda wa Blantyre pamene anali nawo pa mwambo wa mapemphero.

Iwo ati atsogoleri a mipingo akuyenera kulimbikitsa anthu kuti adzifunsa atsogoleri monga nduna za boma ndi aphungu, mwachitsanzo, chifukwa chimene kudera kwawo sakulandira ndalama za Mtukula Pakhomo, mwa zina.

Iwo atinso anthu adzifunsa aphungu awo momwe ndalama za chitukuko cha mmadera (CDF) azigwiritsira ntchito, poganizira kuti mtsogoleri wa dziko lino Dr Lazarus Chakwera anakweza CDF kuchoka pa K40 million kufika pa K100 million kuti chitukuko chidzioneka mmadera.

Wolemba: Arthur Chokhotho

Related posts

Bambo mfumu alimbikitsa anthu kukhala olimbikira pa ntchito za Mulungu

Mayeso Chikhadzula

Khonsolo ya Zomba ndiyokondwa ndi zitukuko

Romeo Umali

Chikho cha K10 million achikhazikitsa m’boma la Chikwawa

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.