Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Thandizani odwala mwa chikondi – AWRIM

Pofuna kuonetsetsa kuti ana, achikulire komanso okalamba akulandira thandizo lachipatala mwaulemu komanso mogwirizana ndi ufulu wawo akapita kuchipatala, bungwe la masisiteli ampingo wa Katolika la Association of Women in Religious Institute of Malawi (AWRIM), kudzera mu AWRIM Health Care Network, lachititsa maphunziro a masiku awiri kwa anthu ogwira ntchito m’zipatala za mpingowu.

Maphunzirowa amapereka upangiri wa momwe angathandizire odwala omwe ali pa chiopsyezo. Maphunzirowa anachitikira mu mzinda wa Lilongwe.

Malinga ndi a Sisiteli Teresa Mulenga omwe akuyendetsa ntchitoyi pansi pa bungwe la AWRIM Health Care Network , nthumwi zomwe zinabwera pa maphunzilowa zikuyembekezeka kukagawana ndi kuphunzitsa anzawo m’zipatala zonse za mpingo wa Katolika m’zigawo zonse dziko lino.

“Taphunzila zambiri monga kulemekeza odwala komanso momwe tingawathandizire malinga ndi ufulu wawo”, anatero Sisiteli Mulenga.

Sisiteli Mulenga anatinso pamaphunzirowa anabweretsa anthu omwe amagwira ntchito za kalembera mzipatalazi kuti adzitha kupanga kalondolondo wa bwino wa anthu omwe umoyo wawo uli pa chiopsyezo.

Mmodzi mwa nthumwi za kumaphunzirowa Sisiteli Lexina Mwale omwe alikuchipatala cha Ludzi ati maphunzirowo ndi ofunika kwambiri ndipo abwera mu nthawi yake.

“Taphunzira zothandiza kwambiri anthu amene miyoyo yawo ili pa chiopsyezo monga ana ndi anthu achikulire komanso okalamba,” anatero Sisiteli Mwale.

Wolemba Glory Chinyanga
#MBCDigital
#Manthu

Related posts

MDF laments high encroachment at its training areas.

MBC Online

Govt. reaffirms no Malawian will die of hunger

Romeo Umali

A Malawi First sachitanso zionetsero zotsutsana ndi chizindikiro cha tax stamp

McDonald Chiwayula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.