Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Politics

Ena otsatira UTM atsutsa zotsatira zachisankho

Mamembala ena a chipani cha UTM ati sakugwirizana ndi zotsatira zachisankho zimene zinachitika ku msonkhano waukulu wa chipanichi sabata yathayi.

Muzisankhozi, a Dalitso Kabambe ndi amene adawasankha kukhala mtsogoleri watsopano pamodzi ndi mamembala ena amene adawasankha maudindo osiyanasiyana.

Kusamvanaku kwadza pamenenso m’modzi mwa amene anapikisana nawo pa udindo wa mtsogoleri wa chipanichi, a Matthews Mtumbuka, anaganizirapo kuti chinyengo chinachitika kuti alephere.

Mu chikalata chimene atulutsa mamembalawa, ndipo asayinira ndi a Charles Kondowe, Kondwani Munthali ndi a Fletcher Katambalare, iwo ati ndi odabwa kuti anthu ena a chipani china anali nawo m’gulu la anthu ovota.

Iwo anatinso anthu onse amene anayambitsa nawo chipanichi sanapeze maudindo akuluakulu ndipo akuganizira kuti anthu ena amene ali m’maudindo atsopanowa anachita kuwatuma ndi a chipani china.

Gulu la anthuwa likugwirizana ndi zimene mtsogoleri wakale wa UTM, Dr Michael Usi, ananena kuti chipanichi sichinatsate ndondomeko zovomerezeka zochitira msonkhano waukulu.

Related posts

Jenda Police nets two unlicensed hemp possessors

Romeo Umali

Journalists urged to prioritise financial responsibility

Rabson Kondowe

Activist applauds Chakwera’s timely declaration of state of disaster

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.