Malawi Broadcasting Corporation
Business Development Local Local News Nkhani

‘Ngongole za NEEF ndiza aliyense’

Wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino, Dr Michael Usi, wati zokambirana zomwe bungwe la NEEF likuchita ndi anthu zikuthandiza kuti anthu amvetse ndikutsatira momwe ngongole ya bungweli ikuyendera.

Dr Usi ayankhula izi pa zokambirana zomwe bungweli lachititsa ndi adindo a m’boma la Blantyre monga mafumu, makhansala, komanso ena mwa aphungu ochokera m’bomali.

Iwo ati ali ndi chiyembekezo kuti anthu oyenera ndiwo adzitenga ngongolezi ndipo anatsindika kuti ngongolezi sizandale koma za a Malawi.

Mkulu wa bungwe la NEEF, a Humphreys Mdyetseni, ati bungweli liri ndi mitundu ya ngongole yokwana 25 zomwe likupereka kwa anthu mdziko muno.

Ndipo mayi Mary Chikopa amene amachita bizinesi yogulitsa nsalu mu msika wa Limbe, ati iwo ndi m’modzi mwa anthu omwe apindula ndi ngongole ya NEEF ndipo ati buzinesi yawo yakula.

Mgawo loyamba la ngongole za NEEF, bungweli linapereka ndalama zokwana K100 billion ndipo posachedwapa, boma linakhazikitsa ndalama zokwana K350 billion zimene likupereka kwa anthu pothetsa umphawi.

Olemba: Mercy Zamawa

Related posts

PRISAM demands arrests over school vandalism

McDonald Chiwayula

Malawi embraces COMESA Yellow Card Scheme for insurance

Rabson Kondowe

Summit of the future consultative meeting underway

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.