Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Politics

Dr Chakwera ndi odekha, a dongosolo — Gotani Hara

Wachiwiri kwa mtsogoleri wa chipani cha Malawi Congress (MCP), a Catherine Gotani Hara, wayamikira mtsogoleri wa chipanichi komanso dziko lino, Dr Lazarus Chakwera, ponena kuti ndiodekha komanso ochita zinthu mwa dongosolo.

Iwo amayankhula izi m’boma la Rumphi pa bwalo la masewero a Polisi ya Rumphi pamene amawatsimikizira anthu okonda chipani cha MCP kuti boma la Dr Chakwera ndi lokonzeka kumalizitsa ntchito zachitukuko zosiyanasiyana m’dziko muno.

A Gotani Hara anakambapo pa nkhani za misewu kuti ntchitozi zikuoneka ngati zikuchedwa malo ena kaamba kakuti boma likufuna kumanga zinthu zolimba zomwe ndi zokomera aMalawi onse pothandiza ntchito zambiri zachitukuko kuphatikizapo malonda.

Olemba: Jackson Sichali

Related posts

SRPC introduces cooperative to promote financial empowerment

Romeo Umali

Chongoni rock art goes digital

Doreen Sonani

Concern over illegal mining in Nkhotakota Game Reserve

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.