Malawi Broadcasting Corporation
Entertainment Local Local News Nkhani

Mwambo wapachaka wa Kungoni Arts and Culture wayamba

Khwimbi la anthu lasonkhana pa Parish ya Mua ku Mtakataka m’boma la Dedza komwe kuli mwambo wapachaka wa Kungoni Arts and Culture Festival.

Ku mwambowu kuli zochitika zosiyanasiyana kuphatikizapo mwambo wa mapemphero, magule a chikhalidwe komanso gulu loyimba nyimbo zachikhalidwe lochokera mdziko la Uganda la Br Jolly Joe Jazz Band.

Mwambowu womwe umachitika kamodzi pachaka umatsogoleredwa ndi akuluakulu a zipembedzo zosiyanasiyana komanso magulu a zachikhalidwe.

Chaka chino, mwambowu ukuchitika pamutu woti “Umwini ndiye maziko a dziko lathu, chimvano cha mavu choning’a pamimba”.

 

Related posts

President Chakwera akayendera ntchito zachitukuko kumpoto

Rabson Kondowe

Lucius anali bwenzi lama Rasta — Ras Jonah

Romeo Umali

MBS donates wheelchairs to Kachere Rehab

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.